23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,
24. Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga,Ndi kunena ndi golidi woyengetsa,Ndiwe cikhazikitso canga;
25. Ngati ndinakondwera popeza cuma canga ncacikuru,Ndi dzanja langa lapeza zocuruka;
26. Ngati ndalambira dzuwa lirikuwala,Kapena mwezi ulikuyenda monyezimira;
27. Ndi mtima wanga wakopeka m'tseri,Ndi pakamwa panga padapsompsona dzanja langa;