13. Ngati ndapeputsa mlandu wa kapolo wanga, kapena wa mdzakazi wanga,Potsutsana nane iwo,
14. Ndidzatani ponyamuka Mulungu?Ndipo pondizonda Iye ndidzamyankha ciani?
15. Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenga iyenso?Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?
16. Ngati ndakaniza aumphawi cifuniro cao,Kapena kutopetsa maso a amasiye,
17. Kapena kudya nthongo yanga ndekha,Osadyako mwana wamasiye;