Yobu 30:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Anawapitikitsa pakati pa anthu,Awapfuulira ngati kutsata mbala.

6. Azikhala m'zigwa za cizirezire,M'maenje a m'nthaka ndi m'mapanga.

7. Pakati pa zitsamba alira ngati buru,Pansi pa khwisa asonkhana pamodzi.

8. Ndiwo ana a opusa, inde ana a anthu opanda dzina;Anawaingitsa kuwacotsa m'dziko.

9. Koma tsopano ndasanduka nyimbo ya oterewo,Nandiyesa nthanthi.

10. Anyansidwa nane, akhala patali ndi ine,Saleka kuthira malobvu pankhope panga.

11. Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza;Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.

Yobu 30