Yobu 30:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Iye anandiponya m'matope,Ndipo ndafanana ndi pfumbi ndi phulusa.

20. Ndipfuula kwa Inu, koma simundiyankha;Ndinyamuka, ndipo mungondipenyerera.

21. Mwasandulika kundicitira nkharwe;Ndi mphamvu ya dzanja lanu mundizunza.

22. Mundikweza kumphepo, mundiyendetsa pomwepo;Ndipo mundisungunula mumkuntho.

23. Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa,Ndi ku nyumba yokomanamo amoyo onse.

24. Koma munthu akati agwe, satambasula dzanja lace kodi?Akati aonongeke, sapfuulako kodi?

Yobu 30