11. Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza;Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.
12. Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.
13. Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.
14. Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.
15. Anditembenuzira zondiopsa,Auluza ulemu wanga ngati mphepo;Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.
16. Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga;Masiku akuzunza andigwira.
17. Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine,Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.
18. Mwa mphamvu yaikuru ya nthenda yanga cobvala canga cinasandulika,Cindithina ngati pakhosi pa maraya anga.