8. Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.
9. Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;
10. Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga.Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.
11. Ndinalekeranji kufera m'mimba?Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?
12. Anandilandiriranji maondo?Kapena mabere kuti ndiyamwe?