Yobu 3:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Autemberere iwo akutemberera usana,Odziwa kuutsa cinjokaco.

9. Nyenyezi za cizirezire zide;Uyembekezere kuunika, koma kuusowe;Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;

10. Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga.Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.

11. Ndinalekeranji kufera m'mimba?Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?

12. Anandilandiriranji maondo?Kapena mabere kuti ndiyamwe?

Yobu 3