1. Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wace, nati,
2. Ha! ndikadakhala monga m'miyezi yapitayi,Monga m'masiku akundisunga Mulungu;
3. Muja nyali yace inawala pamutu panga,Ndipo ndi kuunika kwace ndinayenda mumdima;
4. Monga umo ndinakhala m'masiku anga olimba,Muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga;