Yobu 27:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti moyo wanga wonse ukali mwa ine,Ndi mpweya wa Mulungu m'mphuno mwanga;

4. Milomo yanga siilankhula cosalungama,Ndi lilime langa silichula zacinyengo.

5. Sindibvomereza konse kuti muli olungama;Mpaka kufa ine sinditaya ungwiro wanga.

6. Ndiumirira cilungamo canga, osacileka;Cikhalire moyo ine, mtima wanga sunditonza.

7. Mdani wanga akhale ngati woipa,Ndi iye amene andiukira ngati wosalungama.

8. Pakuti ciyembekezo ca wonyoza Mulungu nciani pomlikhatu Mulungu,Pomcotsera moyo wace?

Yobu 27