3. Pakuti moyo wanga wonse ukali mwa ine,Ndi mpweya wa Mulungu m'mphuno mwanga;
4. Milomo yanga siilankhula cosalungama,Ndi lilime langa silichula zacinyengo.
5. Sindibvomereza konse kuti muli olungama;Mpaka kufa ine sinditaya ungwiro wanga.
6. Ndiumirira cilungamo canga, osacileka;Cikhalire moyo ine, mtima wanga sunditonza.
7. Mdani wanga akhale ngati woipa,Ndi iye amene andiukira ngati wosalungama.
8. Pakuti ciyembekezo ca wonyoza Mulungu nciani pomlikhatu Mulungu,Pomcotsera moyo wace?