Yobu 27:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.

16. Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi,Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;

17. Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18. Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19. Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,

20. Zoopsa zimgwera ngati madzi;Nkuntho umtenga usiku.

21. Mphepo ya kum'mawa Imtenga, nacokaiye;Nimkankha acoke m'malo mwace.

Yobu 27