Yobu 24:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,Sadziwa njira zace,Sasunga mayendedwe ace.

14. Kukaca auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;Ndi usiku asanduka mbala.

15. Ndipo diso la wacigololo liyombekezera cisisira,Ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;Nabvala cophimba pankhope pace.

16. Kuli mdima aboola nyumba,Usana adzitsekera,Osadziwa kuunika.

17. Pakuti iwo onse auyesa m'mawa mthunzi wa imfa;Pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18. Atengedwa ngati coyandama pamadzi;Gawo lao litembereredwa padziko;Sadzalunjikanso njira ya minda yamphesa.

Yobu 24