1. Koma Yobu anayankha, nati,
2. Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa;Kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m'kulemera kwace.
3. Ha! ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu,Kuti ndifike ku mpando wace!
4. Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pace,Ndikadadzaza m'kamwa mwanga ndi matsutsano.