Yobu 22:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu?Aweruza kodi mwa mdima wa bii?

14. Mitambo ndiyo comphimba, kuti angaone;Ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.

15. Udzasunga kodi njira yakale,Anaiponda anthu amphulupulu?

16. Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,Cigumula cinakokolola kuzika kwao;

17. Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?

18. Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;Koma uphungu wa oipa unditalikira.

Yobu 22