13. Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu?Aweruza kodi mwa mdima wa bii?
14. Mitambo ndiyo comphimba, kuti angaone;Ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.
15. Udzasunga kodi njira yakale,Anaiponda anthu amphulupulu?
16. Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,Cigumula cinakokolola kuzika kwao;
17. Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?
18. Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;Koma uphungu wa oipa unditalikira.