8. Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao,Ndi ana ao pamaso pao,
9. Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,Ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.
10. Ng'ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika;Ng'ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.
11. Aturutsa makanda ao ngati gulu,Ndi ana ao amabvinabvina.
12. Ayimbira lingaka ndi zeze,Nakondwera pomveka citoliro.