Yobu 21:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Mukuti, Mulungu asungira ana ace a munthu coipa cace,Ambwezere munthuyo kuti acidziwe.

20. Aone yekha cionongeko cace m'maso mwace,Namwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.

21. Pakuti comsamalitsa nyumba yace nciani, atapita iye,Ciwerengo ca miyezi yace citadulidwa pakati?

22. Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru?Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.

23. Wina akufa, wabiriwiri,Ali cikhalire ndi cipumulire.

24. Mbale zace zidzala ndi mkaka;Ndi wongo wa m'mafupa ace uli momwe.

Yobu 21