Yobu 20:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zace;Iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?

8. Adzauluka ngati loto, osapezekanso;Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.

9. Diso lidamuonalo silidzamuonanso;Ndi malo ace sadzampenyanso.

10. Ana ace adzapempha aumphawi awakomere mtima;Ndi manja ace adzabweza cuma cace.

11. Mafupa ace adzala nao unyamata wace,Koma udzagona naye pansi m'pfumbi.

12. Cinkana coipa cizuna m'kamwa mwace,Cinkana acibisa pansi pa lilime lace;

Yobu 20