Yobu 20:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Kodi sucidziwa ici ciyambire kale lomwe,Kuyambira anaika munthu pa dziko lapansi,

5. Kuti kupfuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha,Ndi cimwemwe ca wonyoza Mulungu cikhala kamphindi?

6. Cinkana ukulu wace ukwera kumka kuthambo,Nugunda pamitambo mutu wace;

7. Koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zace;Iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?

8. Adzauluka ngati loto, osapezekanso;Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.

Yobu 20