Yobu 20:13-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Cinkana acisunga, osacileka,Naoikhalitsa m'kamwa mwace;

14. Koma cakudya cace cidzasandulika m'matumbo mwace,Cidzakhala ndulu ya mphiri mkati mwace.

15. Anacimeza cuma koma adzacisanzanso;Mulungu adzaciturutsa m'mimba mwace.

16. Adzayamwa ndulu ya mphiri;Pakamwa pa njoka padzamupha.

17. Sadzapenyerera timitsinje,Toyenda nao uci ndi mafuta.

18. Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza;Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.

19. Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.

20. Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace,Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.

21. Sikunatsalira kanthu kosadya iye,Cifukwa cace zokoma zace sizidzakhalitsa.

22. Pomkwanira kudzala kwace adzakhala m'kusauka;Dzanja la yense wobvutika lidzamgwera,

23. Poti adzaze mimba yace,Mulungu adzamponyera mkwiyo wace waukali,Nadzambvumbitsira uwu pakudya iye.

24. Adzathawa cida cacitsulo,Ndi mubvi wa uta wamkuwa udzampyoza.

Yobu 20