Yobu 19:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera;Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.

8. Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko,Naika mdima poyendapo ine.

9. Anandibvula ulemerero wanga,Nandicotsera korona pamutu panga,

10. Nandigamula ponsepo, ndipo ndamukatu;Nacizula ciyembekezo canga ngati mtengo.

Yobu 19