7. Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera;Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.
8. Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko,Naika mdima poyendapo ine.
9. Anandibvula ulemerero wanga,Nandicotsera korona pamutu panga,
10. Nandigamula ponsepo, ndipo ndamukatu;Nacizula ciyembekezo canga ngati mtengo.