Yobu 19:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma ndidziwa kuti Mombolo wanga ali ndi moyo,Nadzauka potsiriza papfumbi.

26. Ndipo khungu langa litaonongeka,Pamenepo wopanda thupi langa, ndidzapenya Mulungu;

27. Amene ndidzampenya ndekha,Ndi maso anga adzamuona, si wina ai.Imso zanga zatha m'kati mwanga.

28. Mukati, Tiyeni timlondole!Popeza cifukwa ca mlandu capezeka mwa ine;

29. Mucite nalo mantha lupanga; Pakuti mkwiyo utenga zolakwa za lupanga,Kuti mudziwe pali ciweruzo.

Yobu 19