Yobu 19:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iye anandicotsera abale anga kutali,Ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.

14. Anansi anga andisowa,Ndi odziwana nane bwino andiiwala.

15. Iwo a m'nyumba mwanga ndi adzakazi anga andiyesa mlendo;Ndine wacilendo pamaso pao.

16. Ndikaitana kapolo wanga, sandibwezera mau,Cinkana ndimpembedza pakamwa panga.

Yobu 19