13. Eni mauta ace andizinga,Ang'amba imso zanga, osazileka;Natsanulira pansi ndulu yanga.
14. Andipasula-pasula;Andithamangira ngati wamphamvu.
15. Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa,Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.
16. Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi,Ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;
17. Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga,Ndi pemphero langa ndi loyera.
18. Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,Ndi kulira kwanga kusowe popumira.
19. Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.