Yobu 16:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Eni mauta ace andizinga,Ang'amba imso zanga, osazileka;Natsanulira pansi ndulu yanga.

14. Andipasula-pasula;Andithamangira ngati wamphamvu.

15. Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa,Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.

16. Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi,Ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;

17. Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga,Ndi pemphero langa ndi loyera.

18. Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,Ndi kulira kwanga kusowe popumira.

19. Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.

Yobu 16