10. Iwo anandiyasamira pakamwa pao;Anandiomba pama ndi kunditonza;Asonkhana pamodzi kunditsutsa.
11. Mulungu andipereka kwa osalungama,Nandiponya m'manja a oipa.
12. Ndinali mkupuma, koma anandityola;Inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya;Anandiimika ndikhale candamali.
13. Eni mauta ace andizinga,Ang'amba imso zanga, osazileka;Natsanulira pansi ndulu yanga.
14. Andipasula-pasula;Andithamangira ngati wamphamvu.
15. Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa,Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.