20. Munthu woipa adzipweteka masiku ace onse,Ndi zaka zowerengeka zisingikira woopsa.
21. M'makutu mwace mumveka zoopsetsa;Pali mtendere amfikira wakumuononga.
22. Sakhulupirira kuti adzaturukamo mumdima,Koma kuti lupanga limlindira;
23. Ayendayenda ndi kufuna cakudya, nati, Ciri kuti?Adziwa kuti lamkonzekeratu pafupi tsiku lamdima,
24. Nsautso ndi cipsinjo zimcititsa mantha,Zimlaka ngati mfumu yokonzekeratu kunkhondo;