Yobu 15:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Munthu woipa adzipweteka masiku ace onse,Ndi zaka zowerengeka zisingikira woopsa.

21. M'makutu mwace mumveka zoopsetsa;Pali mtendere amfikira wakumuononga.

22. Sakhulupirira kuti adzaturukamo mumdima,Koma kuti lupanga limlindira;

23. Ayendayenda ndi kufuna cakudya, nati, Ciri kuti?Adziwa kuti lamkonzekeratu pafupi tsiku lamdima,

24. Nsautso ndi cipsinjo zimcititsa mantha,Zimlaka ngati mfumu yokonzekeratu kunkhondo;

Yobu 15