Yobu 15:14-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Munthu nciani kuti akhale woyera,Wobadwa ndi mkazi kuti akhale wolungama?

15. Taona, Mulungu sakhulupirira opatulika ace;Ngakhale m'mwamba simuyera pamaso pace,

16. Koposa kotani nanga munthu wonyansa ndi wodetsa,Wakumwa cosalungama ngati madzi.

17. Ndidzakuonetsa, undimvere;Cimene ndinaciona, ndidzakufotokozera;

18. Cimene adacinena anzeru,Adacilandira kwa makolo ao, osacibisa;

19. Ndiwo amene analandira okha dzikoli,Wosapita mlendo pakati pao;

20. Munthu woipa adzipweteka masiku ace onse,Ndi zaka zowerengeka zisingikira woopsa.

21. M'makutu mwace mumveka zoopsetsa;Pali mtendere amfikira wakumuononga.

22. Sakhulupirira kuti adzaturukamo mumdima,Koma kuti lupanga limlindira;

Yobu 15