18. Ndipo zoonadi, likagwa phiri, latha;Ndi thanthwe lisunthika m'malo mwace;
19. Madzi anyenya miyala;Zosefukira zao zikokolola pfumbi la nthaka;Ndipo muononga ciyembekezo ca munthu.
20. Mumlaka cilakire, napita iye;Musintha nkhope yace, mumuuza acoke.
21. Ana ace aona ulemu osadziwa iye;Napeputsidwa, koma osazindikira za iwo.
22. Koma thupi lace limuwawira yekha,Ndi mtima wace umliritsa yekha.