Yobu 13:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma inu ndinu opanga zabodza,Asing'anga opanda pace inu nonse.

5. Mwenzi mutakhala cete konse,Ndiko kukadakhala nzeru zanu.

6. Tamvani tsono kudzikanira kwanga,Tamverani kudzinenera kwa milomo yanga.

7. Kodi munenera Mulungu mosalungama,Ndi kumnenera Iye monyenga?

8. Kodi mukhalira kumodzi ndi Iye?Mundilimbirana mwa Mulungu.

9. Ncokoma kodi kuti Iye akusanthuleni?Kodi mudzamnyenga Iye monga munyenga munthu?

Yobu 13