Yobu 13:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ukulu wace sukucititsani mantha,Ndi kuopsa kwace sikukugwerani kodi?

12. Zikumbutso zanu ndizo miyambi ya mapulusa;Zodzikanira zanu zikunga malinga adothi.

13. Khalani cete, ndilekeni, kuti ndinene,Condifikira cifike.

14. Ndilumirenji mnofu wanga pamano panga,Ndi kupereka moyo wanga m'dzanja langa?

15. Angakhale andipha koma ndidzamlindira;Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.

16. Iye adzakhalanso cipulumutso canga,Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.

Yobu 13