11. Ukulu wace sukucititsani mantha,Ndi kuopsa kwace sikukugwerani kodi?
12. Zikumbutso zanu ndizo miyambi ya mapulusa;Zodzikanira zanu zikunga malinga adothi.
13. Khalani cete, ndilekeni, kuti ndinene,Condifikira cifike.
14. Ndilumirenji mnofu wanga pamano panga,Ndi kupereka moyo wanga m'dzanja langa?
15. Angakhale andipha koma ndidzamlindira;Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.
16. Iye adzakhalanso cipulumutso canga,Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.