Yobu 12:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kwa okalamba kuli nzeru,Ndi kwa a masiku ocuruka luntha.

13. Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu;Uphungu ndi luntha ali nazo.

14. Taona, agamula, ndipo palibe kumanganso;Amtsekera munthu, ndipo palibe kumtsegulira,

15. Taona atsekera madzi, naphwa;Awatsegulira, ndipo akokolola dziko lapansi.

16. Kwa Iye kuli mphamvu ndi nzeru.Wonyengedwa ndi wonyenga yemwe ali ace.

Yobu 12