11. Pakuti adziwa anthu opanda pace,Napenyanso mphulupulu, ngakhale saisamalira.
12. Koma munthu wopanda pace asowa nzeru,Ngakhale munthu abadwa ngati mwana wa mbidzi.
13. Ukakonzeratu mtima wako,Ndi kumtambasulira Iye manja ako;
14. Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uicotseretu kutali,Ndi cisalungamo cisakhale m'mahema mwako;
15. Popeza pamenepo udzakweza nkhope yako opanda banga;Nudzalimbika osacita mantha;