Yobu 10:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse;Mundidziwitse cifukwa ca kutsutsana nane.

3. Cikukomerani kodi kungosautsa,Kuti mupeputsa nchito yolemetsa manja anu,Ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?

4. Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?

5. Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;

6. Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;

Yobu 10