Yobu 10:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,

12. Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.

13. Koma izi munazibisa mumtima mwamu;Ndidziwa kuti ici muli naco:

14. Ndikacimwa mundipenya;Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.

15. Ndikakhala woipa, tsoka ine;Ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutuwanga;Ndadzazidwa ndi manyazi, Koma penyani kuzunzika kwanga.

16. Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango;Mubweranso ndi kudzionetsera modabwiza kwa ine.

17. Mundikonzeranso mboni zonditsutsa,Ndi kundicurukitsira mkwiyo wanu;Nkhondo yobwereza-bwereza yandigwera.

18. Potero munandibadwitsa cifukwa ninji?Mwenzi nditapereka moyo wanga, lisanandione diso.

19. Ndikadakhala monga ngati sindikadakhala;Akadanditenga pobadwapo kumka nane kumanda.

Yobu 10