20. Kucilamulo ndi kuumboni! ngati iwo sanena malinga ndi mau awa, ndithu sadzaona mbanda kuca.
21. Ndipo iwo adzapitirira obvutidwa ndi anjala, ndipo padzakhala kuti pokhala ndi njala iwo adzadziputa okha, ndi kutemberera mfumu yao, ndi Mulungu wao; ndi kugadamira nkhope zao kumwamba;
22. nadzayang'ana padziko, koma taonani, nkhawa ndi mdima, kuziya kwa nsautso; ndi mdima woti bi udzaingitsidwa.