Yesaya 66:13-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Monga munthu amene amace amtonthoza mtima, momwemo ndidzatonthoza mtima wanu; ndipo mudzatonthozedwa mtima m'Yerusalemu.

14. Ndipo mudzaciona, ndipo mtima wanu udzasangalala, ndipo mafupa anu adzakula ngati msipu; ndipo dzanja la Yehova lidzadziwika ndi atumiki ace, ndipo adzakwiyira adani ace.

15. Pakuti taonani, Yehova adzafika m'moto, ndi magareta ace adzafanana ndi kabvumvulu; kubwezera mkwiyo wace ndi ukali, ndi kudzudzula ndi malawi amoto,

Yesaya 66