1. Mwenzi mutang'amba kumwamba ndi kutsikira pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu;
2. monga pamene moto uyatsa zitsamba, ndi moto uwiritsa madzi; kudziwitsa kwa amaliwongo anu dzina lanu, kuti amitundu anthunthumire pamaso panu,
3. Pamene Inu munacita zinthu zoopsya, zimene ife sitinayang'anira, Inu munatsika, mapiri anagwedezeka pamaso panu.
4. Pakuti kuyambira kale anthu sanamve pena kumvetsa ndi khutu, ngakhale diso silinaone Mulungu wina popanda Inu, amene amgwirira nchito iye amene amlindirira Iye.