Yesaya 63:17-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Yehova bwanji mwatisoceretsa kusiya njira zanu, ndi kuumitsa mitima yathu tisakuopeni? Bwerani, cifukwa ca atumiki anu, mafuko a colowa canu.

18. Anthu anu opatulika anakhala naco kanthawi kokha; adani athu apondereza kacisi wanu wopatulika.

19. Ife takhala ngati iwo amene simunawalamulira konse, ngati iwo amene sanachedwa dzina lanu.

Yesaya 63