17. Yehova bwanji mwatisoceretsa kusiya njira zanu, ndi kuumitsa mitima yathu tisakuopeni? Bwerani, cifukwa ca atumiki anu, mafuko a colowa canu.
18. Anthu anu opatulika anakhala naco kanthawi kokha; adani athu apondereza kacisi wanu wopatulika.
19. Ife takhala ngati iwo amene simunawalamulira konse, ngati iwo amene sanachedwa dzina lanu.