1. Wolungama atayika, ndipo palibe munthu wosamalirapo; ndipo anthu acifundo atengedwa, palibe wolingalira kuti wolungama acotsedwa pa coipa cirinkudza.
2. Iye alowa mumtendere, iwo apuma pa mphasa zao, yense woyenda moongoka.
3. Koma sendererani kuno cifupi, inu ana amuna a watsenga, mbeu yacigololo ndi yadama.