14. Koma Ziyoni anati, Yehova wandisiya ine, ndipo Ambuye wandiiwala ine.
15. Kodi mkazi angaiwale mwana wace wa pabere, kuti iye sangacitire cifundo mwana wombala iye? inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.
16. Taona ndakulembera iwe pa zikhato za manja anga; makoma ako alipo masiku onse pamaso panga,
17. Ana ako afulumira; opasula ako ndi iwo amene anakusakaza adzacoka pa iwe.
18. Tukula maso ako kuunguza-unguza, nuone; onsewa asonkhana pamodzi, nadza kwa iwe. Pali Ine, ati Yehova, iwe ndithu udzadzibveka wekha ndi iwo onse, monga ndi cokometsera, ndi kudzimangira nao m'cuuno ngati mkwatibwi.