2. Iye sadzapfuula, ngakhale kukuwa, pena kumvetsa mau ace m'khwalala.
3. Bango lophwanyika sadzalityola, ndi lawi lozirala sadzalizima; adzaturutsa ciweruzo m'zoona.
4. Iye sadzalephera kapena kudololoka, kufikira atakhazikitsa ciweruzo m'dziko lapansi; ndipo zisumbu zidzalindira cilamulo cace.
5. Atero Mulungu Yehova, Iye amene analenga thambo, nalifutukula, nayala ponse dziko lapansi, ndi cimene cituruka m'menemo, Iye amene amapatsa anthu a m'menemo mpweya, ndi mzimu kwa iwo amene ayenda m'menemo;