Yesaya 42:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Imvani, agonthi inu; yang'anani, akhungu inu, kuti muone.

19. Ndani ali wakhungu, koma mtumiki wanga? pena wagonthi, monga mthenga wanga, amene ndimtumiza? ndani ali wakhungu monga bwenzi langa, ndi wakhungu monga mtumiki wa Yehova?

20. Iwe waona zinthu zambiri, koma susamalira konse; makutu ako ali otseguka, koma sumva konse.

21. Cinakondweretsa Yehova cifukwa ca cilungamo cace kukuza cilamulo, ndi kucilemekeza.

22. Koma awa ndiwo anthu olandidwa zao ndi kufunkhidwa; iwo onse agwa m'mauna, nabisidwa m'nyumba zakaidi; alandidwa zao, palibe wowapulumutsa; afunkhidwa ndipo palibe woti, Bwezerani.

23. Ndani mwa inu adzachera khutu lace pamenepo? amene adzamvera ndi kumva nthawi yakudza?

Yesaya 42