1. Taona Mtumiki wanga, amene ndimgwiriziza; Wosankhika wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; ndaika mzimu wanga pa Iye; Iye adzaturutsira amitundu ciweruziro.
2. Iye sadzapfuula, ngakhale kukuwa, pena kumvetsa mau ace m'khwalala.
3. Bango lophwanyika sadzalityola, ndi lawi lozirala sadzalizima; adzaturutsa ciweruzo m'zoona.
4. Iye sadzalephera kapena kudololoka, kufikira atakhazikitsa ciweruzo m'dziko lapansi; ndipo zisumbu zidzalindira cilamulo cace.