5. Yehova wakwezedwa; pakuti akhala kumwamba; Iye wadzaza Ziyoni ndi ciweruzo ndi cilungamo.
6. Ndipo kudzakhala cilimbiko m'nthawi zako, cipulumutso cambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko cumacace.
7. Taonani, olimba mtima ao angopfuula kunja, mithenga ya mtendere ilira kowawa.
8. Njira zamakwalala zikufa, kulibe woyendamo; Asuri watyola cipangano, wanyoza midzi, sasamalira anthu.
9. Dziko lilira maliro ndi kulefuka; Lebano ali ndi manyazi, nafota; Saroni afanana ndi cipululu; pa Basana ndi Karimeli papukutika.