Yesaya 31:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Aigupto kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magareta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israyeli, ngakhale kumfuna Yehova!

2. Koma Iyenso ali wanzeru, nadzatengera coipa, ndipo sadzabwezanso mau ace, koma adzaukira banja la ocita zoipa, ndi amene athandiza iwo akugwira nchito yoipa.

3. Koma Aaigupto ndiwo anthu, si Mulungu; ndi akavalo ao ali nyama, si mzimu; ndipo pamene Yehova adzatambasula dzanja lace, wothandiza adzapunthwa, ndi wothandizidwa adzagwa, ndipo iwo onse awiri pamodzi adzalephera.

Yesaya 31