12. Anthu anga awabvuta ndi ana, awalamulira ndi akazi. Anthu anga inu, iwo amene akutsogolerani, ndiwo akucimwitsani, naononga njira zanu zoyendamo.
13. Yehova aimirira kuti atsutsane, naimiriranso kuti aweruze mitundu ya anthu.
14. Yehova adzalowa monenera mirandu ndi okalamba a anthu ace, ndi akuru ace: Ndinu amene mwadya munda wamphesa, zofunkha za waumphawi ziri m'nyumba zanu;
15. muti bwanji inu, amene mupsinja anthu anga, ndi kupera nkhope ya wosauka? ati Ambuye Yehova wa makamu.