Yesaya 3:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo onani, Ambuye, Yehova wa makamu, wacotsa ku Yerusalemu ndi ku Yuda mcirikizo wocirikiza cakudya conse ndi madzi onse, zimene zinali mcirikizo;

2. munthu wamphamvu, ndi munthu wankhondo; woweruza, ndi mneneri, ndi waula, ndi nkhalamba;

3. kapitao wa makumi asanu, ndi munthu wolemekezeka, ndi mphungu, ndi mmisiri waluso, ndi wodziwa matsenga.

4. Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akuru ao, mwacibwana adzawalamulira.

Yesaya 3