1. Ndipo onani, Ambuye, Yehova wa makamu, wacotsa ku Yerusalemu ndi ku Yuda mcirikizo wocirikiza cakudya conse ndi madzi onse, zimene zinali mcirikizo;
2. munthu wamphamvu, ndi munthu wankhondo; woweruza, ndi mneneri, ndi waula, ndi nkhalamba;
3. kapitao wa makumi asanu, ndi munthu wolemekezeka, ndi mphungu, ndi mmisiri waluso, ndi wodziwa matsenga.
4. Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akuru ao, mwacibwana adzawalamulira.