10. Kuomba kwanga nanga, ndi za pa dwale langa: cimene ine ndinacimva kwa Yehova wa makamu Mulungu wa Israyeli, ndanena kwa inu.
11. Katundu wa Duma.Wina aitana kwa ine kucokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku?
12. Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.