Yesaya 2:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ndi pa mitengo yonse yamkungudza ya Lebano, yaitari ndi yotukulidwa, ndi pa mitengo yonse yathundu ya Basana;

14. ndi pa mapiri onse atari, ndi pa zitunda zonse zotukulidwa;

15. ndi pa nsanja zazitari zonse, ndi pa macemba onse;

16. ndi pa ngalawa zonse za Tarisi, ndi pa zithunzithunzi zonse zokondweretsa.

17. Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

Yesaya 2