Yeremiya 9:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Atero Yehova wa makamu, Kumbukirani inu, ndi kuitana akazi akulira, adze; aitaneni akazi ocenjera, kuti adze;

18. afulumire, atikwezere ife mau a maliro, kuti maso athu agwe misozi, ndi zikope zathu ziyendetse madzi.

19. Pakuti mau a kulira amveka m'Ziyoni, Tafunkhidwa, tanyazitsidwa, pakuti tasiya dziko, pakuti agwetsa zokhalamo zathu.

20. Koma imvani mau a Yehova, akazi inu, khutu lanu lilandire mau a pakamwa pace, phunzitsani ana anu akazi kulira, ndi yense aphunzitse mnzace maliridwe ace.

Yeremiya 9