9. Ndipo anamgwira iye, namtengera kwa mfumu ya ku Babulo ku Ribila m'dziko la Hamati; ndipo iye anamweruza.
10. Ndipo mfumu ya ku Babulo inapha ana a Zedekiya pamaso pace; niphanso akuru onse a Yuda m'Ribila.
11. Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, ndipo mfumu ya ku Babulo inammanga m'zigologolo, nimtengera ku Babulo, nimuika m'ndende mpaka tsiku la kufa kwace.
12. Mwezi wacisanu, tsiku lakhumi la mwezi, ndico caka cakhumi ndi cisanu ndi cinai ca Nebukadirezara, mfumu ya ku Babulo, analowa m'Yerusalemu Nebuzaradani kapitao wa alonda, amene anaimirira pamaso pa mfumu ya ku Babulo: