Yeremiya 52:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma nkhondo ya Akasidi inamtsata mfumu, nimpeza Zedekiya m'zidikha za ku Yeriko; ndipo nkhondo yace yonse inambalalikira iye.

9. Ndipo anamgwira iye, namtengera kwa mfumu ya ku Babulo ku Ribila m'dziko la Hamati; ndipo iye anamweruza.

10. Ndipo mfumu ya ku Babulo inapha ana a Zedekiya pamaso pace; niphanso akuru onse a Yuda m'Ribila.

11. Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, ndipo mfumu ya ku Babulo inammanga m'zigologolo, nimtengera ku Babulo, nimuika m'ndende mpaka tsiku la kufa kwace.

Yeremiya 52