Yeremiya 5:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ndipo aneneri adzasanduka mphepo, ndipo mwa iwo mulibe mau; comweco cidzacitidwa ndi iwo.

14. Cifukwa cace Yehova Mulungu wa makamu atero, Cifukwa munena mau awa, taona, ndidzayesa mau anga akhale m'kamwa mwako ngati moto, anthu awa ndidzayesa nkhuni, ndipo udzawatha iwo.

15. Taonani, ndidzatengera pa inu mtundu wa anthu akutari, inu nyumba ya Israyeli, ati Yehova; ndi mtundu wolimba, ndi mtundu wakalekale, mtundu umene cinenero cace simudziwa, ngakhale kumva zonena zao.

16. Phodo lao liri ngati manda apululu, onsewo ndiwo olimba.

17. Adzadya zokolola zako, ndi mkate wako, umene ana ako amuna ndi akazi ayenera kudya; adzadya nkhosa zako ndi zoweta zako; adzadya mphesa zako ndi nkhuyu zako; adzapasula ndi lupanga midzi yamalinga yako, imene ukhulupiriramo.

Yeremiya 5